MITU
WERENGANI nyuzipepala ina iliyonse. Onererani TV, kapena mvetserani wailesi. Pali nkhani zambirimbiri za upandu, nkhondo, ndi uchigawenga. Ndiyeno ganizirani mavuto anu. Mwinamwake ndinu wachisoni kwambiri chifukwa chakuti munthu amene mumam’konda akudwala kapena anamwalira. Mungamamve ngati mmene munthu wabwino Yobu anamvera. Yobu ananena kuti “ndakhuta mavuto.”—Yobu 10:15, The Holy Bible in the Language of Today.
Dzifunseni kuti:
Baibulo lili ndi mayankho ogwira mtima a mafunso amenewa.
“Adzawapukutira misozi yonse kuichotsa pamaso pawo; ndipo sipadzakhalanso imfa; ndipo sipadzakhalanso maliro, kapena kulira, kapena chowawitsa.”—Chivumbulutso 21:4
“Wopunduka adzatumpha ngati nswala.”—Yesaya 35:6
“Maso a akhungu adzatsegudwa.”—Yesaya 35:5
“Onse ali m’manda achikumbutso . . . adzatuluka.”—Yohane 5:28, 29, NW
“Wokhalamo sadzanena, Ine ndidwala.”—Yesaya 33:24
“M’dzikomo mudzakhala dzinthu dzochuluka.”—Salmo 72:16
Musafulumire kuganiza kuti zimene zanenedwa ndi maganizo chabe okhumba zinthu zabwino. Mulungu walonjeza kuti adzachita zimenezi, ndipo Baibulo limalongosola mmene adzazichitira.
Koma Baibulo limathandizanso pambali zina. Limafotokoza chinsinsi cha mmene mungakhalire ndi moyo wosangalatsadi ngakhale panopo. Taganizirani kaye zinthu zimene zimakudetsani nkhawa komanso mavuto amene muli nawo. Zimenezi zingakhudze kusowa ndalama, mavuto a banja, kudwala, kapena kumwalira kwa munthu amene mumam’konda. Baibulo lingakuthandizeni kuthana ndi mavuto masiku ano, ndipo lingakutsitsimuleni mwa kuyankha mafunso onga ngati awa:
Kuwerenga buku lino kumene mukuchitaku ndi umboni wakuti mukufuna kudziwa zimene Baibulo limaphunzitsa. Buku lino likuthandizani. Onani kuti ndime iliyonse ili ndi funso lake m’munsi mwa tsamba limenelo. Anthu ambiri aikonda njira yogwiritsa ntchito mafunso ndi mayankho pokambirana za m’Baibulo ndi Mboni za Yehova. Tikukhulupirira kuti inunso muikonda. Mulungu akudalitseni pamene tsopano mukuyamba kuona kusangalatsa kwake kwa kuphunzira zimene Baibulo kwenikweni limaphunzitsa!
M’Baibulo muli mabuku ndi makalata ndipo onse pamodzi amakwana 66. Mabuku ndi makalata amenewa anawagawa m’machaputala ndi mavesi kuti asamavute kupeza. Tikamatchula malemba m’buku lino, nambala yoyambirira kuchokera pa dzina la buku kapena kalata ya m’Baibuloyo ikuimira chaputala, pamene nambala yotsatira yakeyo ikuimira vesi. Mwachitsanzo, tikalemba kuti “2 Timoteo 3:16” zikutanthauza kuti kalata yachiwiri yopita kwa Timoteo, chaputala 3, vesi 16.
Simuchedwa kulizolowera Baibulo ngati muziwerenga m’Baibulolo malemba amene asonyezedwa m’buku lino. Ndiponso, bwanji osakonza pulogalamu yakuti muziwerenga Baibulo tsiku lililonse? Mutati muziwerenga machaputala atatu mpaka asanu pa tsiku, mukhoza kuwerenga Baibulo lonse pakutha chaka.